Mkulu wa bankiyi a Kwanele Mgwenya walengeza izi kwa atolankhani azamasewero mu mzinda wa Blantyre, komwe anati kukweraku ndi kaamba koti bungwe loyendetsa masewero a mpira wamiyendo la FAM likugwira bwino ntchito yake m’dziko muno.
Mlembi wa bungwe la FAM a Alfred Gift Gunda wati ndiokondwa ndi izi.
Ndalamazi pakutha pa mpikisanowu chaka chino azigwilitsa ntchito yotukula maphunziro a asungwana.
Timu za FCB Nyasa Bullets ndi Silver Strikers ndi zomwe zisewere masewerowa chaka chino.