Mzikayo, a Woonja Hwang, inaphedwa pafupi ndi mtsinje wa Lilongwe pomwe imapita kukaphunzira masewero a tenisi ku bwalo la Lilongwe Golf Club.
Anthuwa akuwaganiziranso kuti anaba lamya ya m’manja ya malemuwo.
Wachiwiri kwa mneneri wa apolisi m'dziko lino Superintendent Alfred Chimthere watiuza kuti anthuwa akaonekera m’bwalo la milandu posachedwapa, kukayankha mlandu wokupha.