Standard Bank - BOL to Wallet

Loya Wati Athandiza Mayi waku Mchinji Yemwe Apolisi Anamumanga Pamodzi ndi Khanda Lake

Loya wina Alexious Kamangila ,wadzipereka kuti ayimira mwaulere mayi wa zaka 30 ku Mchinji, yemwe wakhala akusungidwa ndi a polisi pamodzi ndi mwana wake pa mlandu wonyanyalira mwamuna khanda.

A Kamangila, omwe ndi mphunzitsi ku univesite ya Malawi, ati atawerenga nkhani ya maiyu pa Zodiak Online aganiza zomuimilira kuti athandizire chilungamo pa nkhaniyi.

A Matilda Chirwa, omwe pano ali pa belo, dzulo anakawonekera ku khothi komwe wachiwiri kwa Magistrate Anne Simwaka wayimitsa mlandu-wu mpaka lachisanu sabata ya mawa pofuna kulola oyimira boma pa mlanduwu kuti abweretse mboni.

Pakadali pano, magistrate Simwaka wagwirizana ndi pempho la loya-yu kuti mayiyu akamuwunike achipatala, ngati kumangidwa kwake sikunasokoneze kaganizidwe kake komanso umoyo wake poti anali atachira chakumene.

Read 2904 times

Last modified on Thursday, 10/08/2023

Login to post comments

NEWS IN BRIEF

Unknown Man Shoots Himself Dead at Chitipi

Last night a man has shot himself dead at Chitipi…
Read more...

Churches Urged to Pray For Piece Ahead of 2025 Elections

Churches have been urged to pray for the nation and…
Read more...

High Import Tax Humpering Progress of Digital Malawi Project

BengolNet, a contractor in the Digital Malawi project has bemoaned…
Read more...

Lucius Banda's Death a Big Blow to UTM

The UTM party has described the death of Musician- cum…
Read more...

German Ambassador Leads Blood Drive Amid Malawi's Critical Shortage

The German ambassador to Malawi says the persistent shortage of…
Read more...
Go to top
JSN Time 2 is designed by JoomlaShine.com | powered by JSN Sun Framework