Mvula Ipitilira
Nthambi yoona zanyengo m'dziko muno yati palibe nkhawa iliyonse ya ng’amba mwezi uno wa January.
Mneneri wa nthambiyi, a Yobu Kachiwanda, wanena izi potsatira uthenga omwe akuluakulu azanyengo ku Zimbabwe apereka kwa mzika za dzikolo kuti kukhala ng’amba kuyambira Lachisanu sabata yatha mpaka pa 2 Febuluwale.
A Kachiwanda ati ngakhale maiko a Malawi ndi Zimbabwe amakhala ndi nyengo yofanana, dziko lino lipitilira kulandira mvula ya mlingo wochuluka monga momwe analengezera m’mwezi wa September chaka chatha.
Published in: News In Brief
Read 3878 times
Login to post comments