Standard Bank - BOL to Wallet

Apolisi Amanga Woganiziridwa Kutaya Mwana

Apolisi kwa Ngabu m'boma la Chikwawa amanga mai wa zaka 20, Maria Akimu, pomuganizira kuti anataya khanda lake lobadwa kumene usiku wa Lachiwiri.

Wachiwiri kwa mneneri wa polisi m'bomalo, Consitabo Chance Mfune, wati Akimu anathawa atapalamula mlanduwu.

Iye wati apolisi agwira Akimu Lachisanu anthu ena atawatsina khutu za komwe anali.

Maria Akimu ndi ophunzira pa sukulu ya sekondale m'deralo.

Khandalo analitaya m’chimbudzi.

Bambo yemwe amakhala moyandikana ndi msungwanayo akuti anamva khanda likulira m’chimbudzi, ndipo anauza anthu ena omwe anathandizira kulipulumutsa.

Achitapatala adati mwanayo, yemwe ndi wamwamuna, anali kupeza bwino.

A Mfune ati msungwanayo, yemwe amachokera m'mudzi mwa Mwadula m'dera la mfumu yaikulu Ngabu, ayankha mlandu obisa uchembere.

Read 39 times
Login to post comments

NEWS IN BRIEF

Apolisi Amanga Woganiziridwa Kutaya Mwana

Apolisi kwa Ngabu m'boma la Chikwawa amanga mai wa zaka…
Read more...

Rising Suicide: Psychologist Blames Lack on Trust

A top psychologist has blamed the sharp rise in suicide…
Read more...

Tourism Grows as Malawi Launches National Tourism Month

Minister of Tourism Vera Kamtukule says the tourism sector has…
Read more...

Father Boucher Remembered for Preserving Malawian Culture

The departed Catholic priest, father Claude Boucher, has been described…
Read more...

Malawi Chewa Group to Hold Parallel Chifukwato Ceremony

Barely a few days after some the Chewa people led…
Read more...
Go to top
JSN Time 2 is designed by JoomlaShine.com | powered by JSN Sun Framework