Noel Mkubwi

Wa polisi m'modzi wavulala pa chiphwilikiti chomwe chinabuka pa mudzi wa Ganthu kwa mfumu Kayesa mdera la mfumu Lukwa ku Kasungu usiku walachinayi.
Anthu a mmudziwo akuti analanda mfuti pa chipolowecho, chomwe akuti chinadza kaamba koti munthu wina akufuna kuti awasamutse pa mudzipo kuti atsekulepo munda.
Mfumu Kayesa yati anthuwa anakwiya ndi kubwera kwa apolisi pa mudzipo, pa nkhani yomwe akuona kuti akuphwanyilidwa ufulu wawo.
"Mudzi wa Ganthu udayamba mchaka cha 1932, koma m’modzi mwa akubanja la chifumu akufuna abale ake , asuweni asamuke kuti azilimapo zomwe mzolakwika," inatero mfumuyi.
Koma mneneri wa apolisi ku Kasungu a Josephy Kachikho wati nthambi ya za nkhalango inakatenga apolisiwo kuti akathandize kulanda makala ndipo ndi komwe chiphwilikiticho chinabuka.
Iwo atsimikiza za kuvalazidwa kwa wapolisiyo, ndipo anati apolisi akufufuza kuti adziwe msonga yeniyeni ya nkhaniyi.
"Ofesi ya za nkhalango inatifunsa kuti akufuna asilikali kuti akalande makala. Ngati anthuwo akuti ndi nkhani ya malo ndiye kuti tifufuza," atero a Kachikho.
Wapolisi yemwe wavulalazidwa ali mchipatala cha Kasungu ndipo mfuti yomwe anthuwo analanda yapezeka.
Three family members have sustained serious injuries after a wall of their house fell on them at Chisiwiri Village in the area of Senior chief Lukwa in Kasungu on Friday morning.
Three family members have sustained serious injuries after a wall of their house fell on them at Chisiwiri Village in the area of Senior chief Lukwa in Kasungu on Friday morning.
The Department of Parks and Wildlife has expressed satisfaction with the conviction and sentencing of two poachers in Kasungu who have earned themselves seven years and three months each for poaching a buffalo in the protected area.
First-Year University of Malawi Student Shadreck Kamwana has developed an Android software which can control electrical appliances by the command of voice.
At least ten people died in a road accident around Nkhamenya in Kasungu district last night. Three others are critically injured.
The Malawi Police Service says it has no clue on the whereabouts of one of its recruit constables who has been missing for weeks in Kasungu.