Loya Wati Athandiza Mayi waku Mchinji Yemwe Apolisi Anamumanga Pamodzi ndi Khanda Lake

Loya wina Alexious Kamangila ,wadzipereka kuti ayimira mwaulere mayi wa zaka 30 ku Mchinji, yemwe wakhala akusungidwa ndi a polisi pamodzi ndi mwana wake pa mlandu wonyanyalira mwamuna khanda.

A Kamangila, omwe ndi mphunzitsi ku univesite ya Malawi, ati atawerenga nkhani ya maiyu pa Zodiak Online aganiza zomuimilira kuti athandizire chilungamo pa nkhaniyi.

A Matilda Chirwa, omwe pano ali pa belo, dzulo anakawonekera ku khothi komwe wachiwiri kwa Magistrate Anne Simwaka wayimitsa mlandu-wu mpaka lachisanu sabata ya mawa pofuna kulola oyimira boma pa mlanduwu kuti abweretse mboni.

Pakadali pano, magistrate Simwaka wagwirizana ndi pempho la loya-yu kuti mayiyu akamuwunike achipatala, ngati kumangidwa kwake sikunasokoneze kaganizidwe kake komanso umoyo wake poti anali atachira chakumene.

Read 1875 times

Last modified on Thursday, 10/08/2023

Login to post comments

NEWS IN BRIEF

BREAKING: John Tembo Dies

Former Malawi Congress Party president and veteran politician John Zenus…
Read more...

Mass Polio Vaccination Campaign Surpasses Target

Preliminary figures for the second round of mass polio vaccination…
Read more...

Min. of Education to Engage Reps of Unemployed Primary School Teachers

The ministry of education has today called representatives of some…
Read more...

MCTU Introduces New Project to End Child Labour

The Malawi Congress of Trade Union (MCTU) has introduced a…
Read more...

Scores of Children Fail to Start School in Machinga

At least 38 children have today failed to return to…
Read more...
Go to top
JSN Time 2 is designed by JoomlaShine.com | powered by JSN Sun Framework